Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Sports Sports

‘Masewero opalasa njinga ali ndi tsogolo’

Unduna wa zamasewero wati ndi okondwa ndi luso limene laoneka pa mpikisano opalasa njinga ku Lilongwe, pamene bungwe la African Union Sports Council of Region 5 likukondwelera kuti lakwanitsa zaka 25.

Mlembi mu undunawu, a Chikumbutso Mtumodzi, anati boma liyesetsa kuthandiza masewerowa kudzera ku bungwe lowayendetsa la Cycling Federation of Malawi.

A Mtumodzi anati izi zili chomwechi chifukwa awona kuti masewerowa ali ndi tsogolo lowala ngati patakhala chidwi cha chikulu chowatukula kuchokera ku makampani komanso anthu osiyanasiyana akufuna kwabwino.

Pampikisanowu, a Peter Zulu ndi amene apambana atapalasa njinga pa mtunda wa makilomita 100 ndipo walandira mphotho yaikulu ya K600, 000.

A Rashid Aufi wakhala kwatswiri pa mtunda wa makilomita 50 ndipo walandira K300, 000.

Olemba: Batuel Gerald

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Namondwe sakhalapo koma mvula yamphamvu m’madera ena — MET

MBC Online

Over 600,00 tree seedlings planted in Chiradzulu

MBC Online

MEC CHAIRMAN TO HOLD PUBLIC LECTURE AT MZUNI

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.