Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Sports Sports

‘Masewero opalasa njinga ali ndi tsogolo’

Unduna wa zamasewero wati ndi okondwa ndi luso limene laoneka pa mpikisano opalasa njinga ku Lilongwe, pamene bungwe la African Union Sports Council of Region 5 likukondwelera kuti lakwanitsa zaka 25.

Mlembi mu undunawu, a Chikumbutso Mtumodzi, anati boma liyesetsa kuthandiza masewerowa kudzera ku bungwe lowayendetsa la Cycling Federation of Malawi.

A Mtumodzi anati izi zili chomwechi chifukwa awona kuti masewerowa ali ndi tsogolo lowala ngati patakhala chidwi cha chikulu chowatukula kuchokera ku makampani komanso anthu osiyanasiyana akufuna kwabwino.

Pampikisanowu, a Peter Zulu ndi amene apambana atapalasa njinga pa mtunda wa makilomita 100 ndipo walandira mphotho yaikulu ya K600, 000.

A Rashid Aufi wakhala kwatswiri pa mtunda wa makilomita 50 ndipo walandira K300, 000.

Olemba: Batuel Gerald

Related posts

FIRST CAPITAL BANK LAUNCHES 5 MITA IPITE PROMOTION

McDonald Chiwayula

Ntchito yonyamula zovuta ku Chikangawa yayambika

MBC Online

Churches urged to reach out to those affected by hunger

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.