Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

MANEPO idzudzula mchitidwe wa nkhanza kwa achikulire

Bungwe la Malawi Network of Older Persons’ Organizations (MANEPO) lati ndi lokhudzidwa ndi kuchuluka kwa nkhanza zomwe achikulire akukumana nazo m’dziko muno kuphatikizapo kuwaganizira kuti ndi mfiti.

Mkulu wa bungweli, a Andrew Kavala amathilirapo ndemanga pa nkhanza zomwe zachitikira  mayi Mary Laini  a zaka  87 a mmudzi mwa  Matewere kwa T/A Juma m’boma la Mulanje pomwe awanamizira kuti amamanga mvula.

A Kavala anati izi ndi kaamba ka umbuli komanso zikhulupiliro zopanda ntchito kuphatikizapo nkhani za ufiti zomwe anati ndi kuphwanya ufulu wa  achikulire m’dziko muno.

M’chikalata chomwe atulutsa a bungwe la MANEPO, apempha a polisi kuti afufuze nkhaniyi ndi kumanga onse okhudzidwa, komanso kuyika ndondomeko zothandiza kuteteza ufulu wa achikulire m’dziko muno.

A bungweli ati akutsatira ndi chidwi kuti chilungamo chiwoneke kwa mayi Laini.

 

Olemba: Grant Mhango

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Silver Strikers eliminates Bullets’ title defence hopes

Romeo Umali

Police Officer, child killed in road accident

Romeo Umali

MAIIC yapanga phindu lokwana K2.5 billion mu 2023

Justin Mkweu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.