Mayi wa pfuko lino, Madam Monica Chakwera, athokoza bungwe la Press Trust pochirimika pa ntchito zotukula maphunziro m’dziko muno.
Madam Chakwera anena izi ku Chiyola mdera la Mwazisi m’boma la Rumphi pamene amatsegulira sukulu ya sekondale yoyendera ya Chiyola imene bungwe la Press Trust lamanga.
Iwo anayamikiranso bungweli pomanga sukulu zambiri m’dziko muno komanso malo ogonenera atsikana zimene ati zikutukula maphunziro.
Madam Chakwera ati kuchuluka Kwa chiwerengero cha anthu mdziko muno kwaonjezeranso vuto la kusowa kwa malo abwino ophunzirira m’sukulu zosiyanasiyana zimene ati boma silingathe kumanga pa kamodzi.
Mayi wa pfukoyi analimbikitsanso atsikana kuti asathamangire banja koma m’malo mwake aphunzire kuti adzakhale odzidalira pawokha komanso agwiritse ntchito mwayi wa sukuluyi kuti akonze tsogolo lawo.