Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Lekani kusala ndi kuchitira nkhanza anthu omwe ali khungu lachi alubino’

Mabungwe olimbikitsa ufulu, YONECO ndi Standing Voices akuyenda m’misika m’madera osiyanasiyana kuphunzitsa anthu za kuipa kosala ndi kuchitira nkhanza anthu omwe ali ndi khungu la chialubino.

M’boma la Mulanje aphunzitsa  anthu m’misika ya kwa Chonde, ku Limbuli ndi kwa Chinakakana kudzera mu zisudzo ndi magule.

Kwa Chinakanaka, mkulu oona zophunzitsa za ufulu ku bungwe la YONECO, a Titus Linzi ati anthu a chialubino akuphwanyiridwa ufulu mu njira zambiri zomwe anthu sadziwa kuti ndi kulakwira malamulo, ndipo kuti atha kulowa nazo kundende.

“Nkhanzazi  ndi monga   kuwakaniza kumanga ukwati,  kuwatchula maina achipongwe monga napweri, pangolini, tomato wapachulu, zigoma. Palinso nkhanza zomwe zimaayamba chifukwa cha zikhulupiriro za bodza,” atero a Linzi.

Ntchitoyi akuitcha Ufulu Wanga Caravan Tours.

Related posts

Stop giving handouts to street kids – Brothers in Arms

MBC Online

How Actellic-treated fish from Nkhata Bay ends up on your plate

Romeo Umali

Four dead in Mzimba road accident

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.