Malawi Broadcasting Corporation
Education Local Local News Nkhani

‘Lekani kugwilira ana’

Aphunzitsi ndi anthu ena oyang’anira ana awachenjeza kuti alekeletu mchitidwe ogwilira ana kupanda kutero lamulo ligwira ntchito.

M’modzi mwa akuluakulu ku unduna oona kuti pasamakhale kusiyana pakati pa amayi ndi abambo, a Chikondi Chiumbudzo Mponda, apereka chenjezoli pamwambo opereka masatifiketi kwa alezi amene amaliza maphunziro awo pansi pampingo wa CCAP Livingstonia Synod m’boma la Mzimba.

A Mponda ati ndi zomvetsa chisoni kuti m’malo moyang’anira ana, aphunzitsi ena akumawagwilira zimene anati ndi zobwezera m’mbuyo ntchito yoteteza ana.

“Posachedwapa aphunzitsi atatu amangidwa chifukwa chogwilira ana, izi ndi zodandaulitsa chifukwa anawa amakhala m’manja mwawo ndipo boma sililekelera mchitidwe otero,” a Mponda anatero.

Mkulu oona za maphunziro a m’mera mpoyamba ku nthambi yampingo wa CCAP Livingstonia Synod, Reverend Nancy Chunga, anati ngakhale pali zovuta zina, ntchito yolimbikitsa maphunziro a m’mera n’poyamba ikuyenda bwino kumpingowu.

Olemba: Henry Haukeya

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

THE DEAD AND NEGLECTED DAMS OF BLANTYRE

MBC Online

19-year-old arrested over murder

Romeo Umali

Kineo & Aidfest to release debut EP

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.