Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Kulowetsa galimoto mozemba ndi mlandu

Bungwe lotolera misonkho la Malawi Revenue Authority MRA lati likukumana ndi mavuto pa ntchito yotolera misonkho, maka pa galimoto zimene zimalowa m’dziko muno mozemba.

Mkulu wazamalonda ku bungweli, a Wilma Chalulu, wati anthu ena samafuna kuti galimoto zawo azifufuze ngati analipira msonkho kapena ayi polowa m’dziko muno.

A Chalulu apempha olembankhani kuti athandize kudziwitsa anthu zakufunika kopereka msonkho pa galimoto polowa mdziko muno komanso kupereka mpata ku bungweli kugwira ntchito mosavuta yofufuza galimoto zamtunduwu.

Boma limagwiritsa misonkho munjira zosiyanasiyana monga kumanga misewu, sukulu, zipatala, nyumba za ogwira ntchito m’boma komanso kupereka malipiro awo.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

‘Nyumba yamalamulo ya ana ikufunika thumba lapadera’

Lonjezo Msodoka

Wapha mwana wa zaka zitatu chifukwa chodutsa mmunda mwake

MBC Online

Apolisi agwira mbala zomwe zinaba katundu wa Radio Maria

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.