Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani Technology

Kaneneni ku Polisi anthu akakulakwirani pa Intaneti — MACRA

Bungwe la MACRA la limbikitsa a Malawi kuti adzikamang’ala ku Polisi ngati anthu ena awalakwira kapena kuwachitira upandu pa masamba a mchezo komanso malo ena pa makina a intaneti, mkulu wa bungweli a Daudi Suleiman anatsimikiza.

Mkulu wa Nthambi ya Computer Emergency Response Team (CERT) ku MACRA, a Christopher Banda, ati izi zikudza pamene madando akuchuluka okhudza anthu amene amachita malonda komanso kuwonetsa luso lawo pa makinawa kuti a Polisi sakumathandiza mokwanira powateteza, zomwe zikuchititsa kuti ntchito yawo isapite patsogolo.

Mwa maupandu ena, ndi monga kutsegula ma accaount abodza pa masamba a mchezo ndi cholinga chofuna kuna,iza, kunyoza komanso kubera ndalama anthu osadziwa.

Olemba : Yamikani Makanga

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Komiti ya COVID 19 siyinayankhulebe pa malipoti akubuka kwa nthendayi

Davie Umar

WHO DONATES ESSENTIAL DRUGS TO MALAWI

Mayeso Chikhadzula

LWB bails out Bwaila Hospital with water tank

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.