Bungwe lotolera misonkho la Malawi Revenue Authority (MRA) lalangiza anthu amene ali ndi galimoto zawo pachipata cha Songwe Border Post kuti akaombole galimotozi ati chifukwa chakuti zikutha malo pamalowa.
Mmodzi wa akuluakulu ku bungweli, a Steven Kapoloma, ati pamalowa pali galimoto zambiri.
“Anthu ambiri anagula galimoto kunja ndipo zitafika akulephera kuwombola, zomwe zikuchititsa kuti malo ano adzadze galimotozi,” a Kapoloma anafotokoza.
Iwo anapempha anthu kuti adzifufuza bwino bwino patsamba lawo ndikuwerengera ndalama zimene zikufunikira kuti awombole galimoto yawo asanayitanitse.
A Kapoloma alangiza anthu kuti atengere mwayi wadongosolo loti akhoza kumalipira ndalama zowombolerazi pang’onopang’ono akangoyitanitsa kuti asamapanikizike.
Olemba: Henry Haukeya

