Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Chikho cha K10 million achikhazikitsa m’boma la Chikwawa

Mmodzi mwa makhumutcha  ochita malonda kwa Ngabu m’boma la Chikwawa Saeed Dinyelo lero wakhazikitsa chikho cha mpira wa miyendo cha ndalama zokwana K10 million.

Mwambowu unachitikira pa bwalo Ngabu Community m’bomalo.

Mmawu ake,  Dinyelo anati wachita izi pamene  ali ndi masomphenya oti derali lidzatulutse timu yomwe idzasewerere mu TNM Super League mtsogolomu.

Mmodzi mwa akuluakulu a bungwe loyendetsa masewero a mpira wa miyendo mdziko muno la FAM, a Daud Mtanthiko ayamikira a Dinyelo pothandizira kupititsa patsogolo masewerowa mdziko muno.

Phungu wa chipani cha MCP wa  delari a Illias Karim anali nawonso pa mwambowu

Matimu okwana 32 ndi omwe atenge nawo mbali mu mpikisanowu.

Pamasewero okhazikitsa chikhochi, timu ya Mapoliko yagonjetsa  Chimpambana Red Tigers ndi zigoli zitatu kwa ziwiri.

 

Olemba Nobert Jameson

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

‘Demanding fees from patients is illegal’

Austin Fukula

Legislators commend MRA on tax stamps initiative

McDonald Chiwayula

Mulhakho wa Alhomwe to elect new members on 2 March

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.