Malawi Broadcasting Corporation
Development Environment Local Local News Nkhani

Bungwe la Clean Cities lalimbikitsa ukhondo ku Lilongwe

Bungwe la Clean Cities Project pamodzi ndi khonsolo ya mzinda wa Lilongwe m’mawa uno likuyenda ulendo wa ndawala umene akutola zinyalala ndi kulimbikitsa anthu kuti adzikhala a ukhondo mu mzindawu.

Martin Manyozo, amene ali mkulu wa bungweli, wati ulendo umenewu ndi ofunikira kwambiri chifukwa uthandiza mzinda wa Lilongwe kuchepetsa chiopsyezo cha matenda a Cholera.

“Chidwi chathu chili pofuna kupereka uthenga koma tikudziwa kuti uthenga paokha siokwanira koma tichitepo kanthu nkuona tikusesa nkutoleranso zinyalala,” anatero a Manyozo.

Ntchitoyi akuyigwira mothandizidwa ndi bungwe la Waste Management komanso ma bungwe ena osiyanasiyana ku phatikizapo a European union, New restoration plan Malawi komanso Waste advisors.

Olemba ndi Kujambula: Paul Mlowoka ndi Margaret Mapando

Related posts

Mwakifwamba Youth Club advocates for a clean environment

Romeo Umali

MBTS yati sikutolera magazi okwanira

Alinafe Mlamba

ACB, Mzimba CSOs sign MOU to fight corruption

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.