Bungwe la Teachers Council of Malawi (TCM) lati pofika pa 1 April chaka chino lamulo ligwira ntchito kwa aphunzitsi amene sapezeka mu kaundula yemwe bungweli likuchititsa.
Aphunzitsiwa ndi a sukulu za mkombaphala, pulayimare, sekondare komanso ophunzitsa aphunzitsi.
M’modzi mwa akuluakulu ku unduna wa za maphunziro, Professor Golden Msilimba, ndi amene anena izi pa msonkhano wa olembankhani munzinda wa Lilongwe.
A Msilimba ati pakadalipano aphunzitsi oposa 93,000 ndi amene akufuna kulembetsa m’kaundulayu ndipo 42,000 akufuna ziphaso.
56,000 mwa iwo akufuna kulembetsa kugwiritsa ntchito mapepala ndipo 37,000 akufuna kulembetsa kudzera pa makina a internet.
Mkulu wa TCM, a Grace Mphandamkoko, ati kuchuluka kwa aphunzitsi ofuna kulembetsa pa mapepala kwachulutsa ntchito ya bungweli chifukwa aphunzitsi ambiri a pulayimare omwe anaphunzira zaka zam’mbuyomu sakudziwa kugwiritsa ntchito ndondomeko za luso la makono.
Komabe, a Msilimba anatsindika kuti unduna uchilimika kuphunzitsa aphunzitsi oterowa kudzera mu ndondomeko ya Continuous Professional Development kuti athe kuthandiza aphunzitsi omwe sakutha kugwiritsa ntchito njira za makonozi.