Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Bambo agwililira mwana

Apolisi ku Lilongwe amanga a Symon Josephy, 35, powaganizira kuti anagwililira mwana wa zaka zisanu ndi zinayi (9) yemwenso ndi mchemwali wa mkazi wa bamboyo.

Wachiwiri kwa ofalitsa nkhani za polisi ya Lilongwe, a Khumbo Sanyiwa, ati bamboyo anapita komwa mowa kumene anabwerako usiku ndipo atafika anapeza mkazi wake wagona. Kenako anapita kuchipinda komwe amagona mwanayo ndi kumugwililira.

A Sanyiwa anati mkazi wa bamboyo atapita ku chipinda cha mwanayo kuti akamuone, anadabwa kuti mwanayo wagwiliridwa. Atamufunsa, bamboyo anavomera kuti wachita izi ndi iyeyo.

A Josephy amachokera m’mudzi wa Sitenala, mfumu yaikulu Mpemba ku Dedza ndipo akaonekera kubwalo lamilandu posachedwapa pa mlandu ogwililira.

 

Related posts

Dietary modifications vital in combating prostate cancer

Romeo Umali

Level 1 Hockey Coaching Course commences in Blantyre

Romeo Umali

Delegates strategise on small-scale fisheries action plan

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.