Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Amuna ambiri kumpoto akudwala khansa ya chida cha abambo

Akuluakulu apa chipatala chachikulu cha Mzuzu ati chipatalachi chikulandira abambo pafupifupi 60 mwezi uli ofuna chithandizo cha nthenda ya khansa ya chida cha abambo, penile cancer mchingerezi.

Malinga ndi Dr Alex Khombedza yemwe amayang’anira ntchito zamdulidwe pa chipatalachi, ambiri mwa abambowa ndi ochokera mzipatala zosiyanasiyana m’chigawo chakumpoto ndipo amafika zinthu zitaonongeka kale kaamba koti nthendayi imayamba ndi timatuza tomwe timanka tikula kutsogolo kwa chida cha abambo.

Dr Alex Khombedza, Mzuzu Central Hospital

Pa tsiku, chipatalachi chimalandira odwala matendawa awiri kapena atatu ndipo Dr Khombedza ati mdulidwe ndi njira yomwe ingathandize polimbana ndi vutoli.

Iwo amalankhula pamaphunziro a olembankhani m’chigawo chakumpoto amene anakonza ndi bungwe la JournAids linakonza ku Mzuzu.

Olembankhani omwe anatenga nao gawo pa maphunzirowa

Pakanali pano katswiri pa nkhani za umoyo George Jobe wati mpofunika kuti ma uthenga okhudza nthendayi afikile pali ponse pofuna kuteteza abambo ambiri ku nthendayi.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Anthu ena akusowabe pokhala – Paramount Chief Kaduya

MBC Online

Mwambo wachionetsero cha zokopa alendo wayamba

Madalitso Mhango

Tilimbikitse ufulu wa anthu omwe ali ndi ulumali— MACODA

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.