Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Amai atatu ali mchitokosi pamulandu wakuba ku Mangochi

Apolisi ku Mangochi amanga amai atatu powaganizila kuti anaba zigubu za oilo wa galimoto mu sitolo ya Chipiku.

Ofalitsa nkhani za polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daudi, auza MBC kuti amaiwa ndi a Diana Thukuwa azaka 60, a Rose Samson azaka 66 komanso ndi a Lucy Mangani azaka 64.

“Malipoti omwe tili nawo ndi okuti pa 2 January chaka cha 2025 amai atatuwa analowa mu sitoloyi ndikuba katunduyu koma mmodzi mwa ogwira ntchito mu sitoloyi ndi amene anawazindikira kuti atulutsa katundu mokuba,” atero a Daudi.

Iwo atinso malipoti apolisi akuonetsanso kuti a Thukuwa adakhalapo ku ndende zaka ziwiri pamulandu ngati omwewu pamene a Samson adawamanga mwezi watha atawagwira atabanso mu sitolo ina yogulitsa katundu osiyanasiyana.

Atatuwa akaonekera kubwalo lamilandu kukayankha mulandu okuba.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Sheriffs seize Bullets’ bus over K25 million debt

MBC Online

Chakwera attending memorial service for late Namibian President Hage Geingob

MBC Online

Karonga concludes league home fixtures in style

Rudovicko Nyirenda
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.