Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

‘Akabaza kalembetseni m’kaundula wa voti’

Mtsogoleri wa Kabaza Association of Malawi (KAMA), a Joseph Petulo, wapempha mamembala awo amene ndi akabaza oposa 3.8 million, kuti apatule nthawi yawo ndi kupeza mpata okalembetsa m’kaundula wa voti.

Iwo ayankhula izi pomwe gawo lachitatu lakalemberayu likupita kumapeto.

“Nthawi zina akabaza ambiri amagwira ntchito kuyamba m’mawa mpaka mdima. Siyani njingayo kaye kalembetseni,” a Petulo anatero.

Iwo anachenjezanso akabaza kuti asamamwe bibida pantchito komanso adzipewa kutenga anthu okayikitsa ndi kuyenda usiku.

“Wakufa savota, utha kukalembetsa koma kufa chifukwa changozi zopeweka, tisamale munyengo yakhirisimisiyi ndi nyuwere,” iwo anatero.

Gawo lachitatu lakalembera linayamba pa 28 November chakachino ndipo litha pa 11 December chakachino.

 

Related posts

POLICE APPREHEND HEALTH WORKER OVER ALLEGED RAPE

MBC Online

Child labour elimination project concludes this December

Alinafe Mlamba

Parliament approves K5.9 trillion National Budget

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.