Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Abambo awiri awapeza olakwa pamulandu wosakaza nkhalango

Bwalo la Senior Grade Magistrate ku Blantyre lachiwiri lapeza olakwa abambo awiri komanso kuwalanda belo chifukwa chopalamula milandu yozembetsa zinthu zamu nkhalango yotetezeka.

Amuna awiriwa  omwe ndi a Jonasi Billiat ndi Evison Michael akuyankha milandu yozembetsa zinthu zamu nkhalango ya boma komanso kupezeka ndi zinthuzo popanda zikalata zachilolezo.

Malinga ndi omwe atsina khutu MBC Digital amuna awiriwa mwezi wa December m’chaka cha 2023 adawagwira ndi matumba 205 amakhala pamalo  wochitila chipikisheni apolisi a GDC roadblock mbandakucha.

Poyankhula mbwaloli wapolisi woimila  boma pa mlandu, Levison Mangani anati sikoyamba a Billiat kupezeka ndi mlandu otere.

Iwo anauza bwaloli kuti mwezi wa April mchaka cha 2021 abambowa  adawapezanso olakwa pamlandu ngati omwewu ndipo adapeleka chindapusa cha K200,000 ndipo galimoto zawo ziwiri adaziombola ndi ndalama zokwana K400,000.

Wapolisi woimila bomayi  anapemphanso kuti galimoto zomwe anagwilitsa ntchito popalamula mlanduwu azilande kaamba koti zikuthandizila kupalamula mlandu.

Pakadali pano, Senior Grade Magistrate M’manga akuyembekezeka kupeleka chigamulo pamlanduwu Lachisanu pa 17 January 2025.

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Maranatha yatumiza ana ambiri ku sukulu za ukachenjede

Simeon Boyce

A Chakwera acheza ndi ochita malonda kunyumba ya boma

MBC Online

NUCLEAR ENERGY SOLUTION FOR ECONOMIC PROGRESS – ZIKHALE NG’OMA

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.