Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Apha makwacha ndi ulimi wamakono wa mpunga

Alimi ang’ono ang’ono olima mpunga omwe amagwilira ntchito mmagulu kwa Maganga m’boma la Salima akuyembekezera kupha makwacha ndi ulimi wamakono wa mpunga kutsatira kuchita bwino kwa mbewu yawo kudzera mu upangiri wa bungwe la African Institute of Corporate Citizenship (AICC).

Alimiwa ati akusiyanitsa phindu lomwe akupeza chiyambileni ulimi wamakonowu kaamba kakuti mbewu yawo ikuchita bwino ngakhale ambiri akhudzidwa ndi mavuto a kusintha kwa nyengo.

Bungwe la AICC limapereka maphunziro akalimidwe ka makono ndi luso pofuna kuti alimi apeze phindu lochuluka pa zolima zawo.

Mkulu wa bungweli, a Driana Lwanda, wati ulimi wampunga wamakono ndi opindulitsa chifukwa umasungira madzi amene amathandiza mbewu kuchita bwino posatengera mavuto odza kaamba ka kusintha kwa nyengo monga ng’amba.

 

Bungwe la AICC likugwira ntchitoyi ndi thandizo la ndalama lochokera ku bungwe la We Effect.

Related posts

Apolisi agwira akuba amenenso anagwililira ophunzira ku Domasi Institute College

Romeo Umali

Khonsolo ya mnzinda wa Zomba ili ndi Mfumu yatsopano

Alinafe Mlamba

Kodi ndi Arsenal kapena Manchester City?

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.