Malawi Broadcasting Corporation
Business Local Local News Nkhani

MBS itsekula sitolo zotsatira malamulo

Ofalitsa nkhani ku bungwe la Malawi Bureau of Standards (MBS), a Wazamazama Katatu, ati bungweli likutsegula sitolo zimene eni ake awaitana kuti akonza mavuto amene analipo.

A Katatu ati sitolozi aziunikanso ngati zakwaniritsa kufikira ndondomeko za ukhondo zimene bungweli limafuna.

Iwo ati sitolo zimene sizikwaniritsa malamulo a ukhondo ndi mfundo za bungweli zikhala chitsekere mpakana pamene atakonze mavutowa.

Mkulu wa sitolo ya Panda ku Area 49 mumzinda wa Lilongwe, a Aaron Mkwezalamba, anati iwo akonza mavuto onse amene analipo m’sitolo yawo monga kupenta komanso kuchotsa mafiliji oonongeka, mwa zina.

A Mkwezalamba ati kuyendera kwa bungwe la MBS mu sitolo yawo kwa waunikira zina zimene samadziwa ndipo ati aonetsetsa kuti akutsata malamulo a ukhondo a bungweli kupita chitsogolo.

Kufikila lero m’mawa, MBS yalandira pempho kuchokera kusitolo zinayi zomwe zinatsekedwa Lolemba kuti akaziyenderenso.

Related posts

Kunkuyu urges COMESA to boost rural internet access

Rabson Kondowe

Truck kills five children

Romeo Umali

Lilongwe Golf Club lifts 2025 Ethco Ladies

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.