Malawi Broadcasting Corporation
Business Local Local News Nkhani

MBS itsekula sitolo zotsatira malamulo

Ofalitsa nkhani ku bungwe la Malawi Bureau of Standards (MBS), a Wazamazama Katatu, ati bungweli likutsegula sitolo zimene eni ake awaitana kuti akonza mavuto amene analipo.

A Katatu ati sitolozi aziunikanso ngati zakwaniritsa kufikira ndondomeko za ukhondo zimene bungweli limafuna.

Iwo ati sitolo zimene sizikwaniritsa malamulo a ukhondo ndi mfundo za bungweli zikhala chitsekere mpakana pamene atakonze mavutowa.

Mkulu wa sitolo ya Panda ku Area 49 mumzinda wa Lilongwe, a Aaron Mkwezalamba, anati iwo akonza mavuto onse amene analipo m’sitolo yawo monga kupenta komanso kuchotsa mafiliji oonongeka, mwa zina.

A Mkwezalamba ati kuyendera kwa bungwe la MBS mu sitolo yawo kwa waunikira zina zimene samadziwa ndipo ati aonetsetsa kuti akutsata malamulo a ukhondo a bungweli kupita chitsogolo.

Kufikila lero m’mawa, MBS yalandira pempho kuchokera kusitolo zinayi zomwe zinatsekedwa Lolemba kuti akaziyenderenso.

Related posts

Beit CURE Malawi appeals for K310 million to heal more children

Romeo Umali

Self-help initiatives springing up in Mwanza

Alinafe Mlamba

CENTRE FOR AGRICULTURAL TRANSFORMATION BAGS INTERNATIONAL AWARD

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.