Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Sports Sports

Zavuta ku Tunisia!

Malawi yagonja 2-0 ndi Tunisia pa bwalo la masewero la Stade Olympique Hammadi Agebri munzinda wa Tunis. Awa anali masewero a mpira wamiyendo odzigulira malo mumpikisano wa 2026 World Cup.

Zigoli za Tunisia adamwetsa ndi Seifeddine Jaziri pamphindi 86 ndi Elias Achouri pamphindi 90+2 kudzera pa penote. Osewera wa Malawi, Lloyd Aarod, adapatsidwa Red Card mu mphindi 64.

Mwayi wa Flames unapezeka pa mphindi 90+8 kudzera pa penate koma ikakuona litsiro siikata, goloboyi wa Tunisia, Aymen Dahmen, anakwanitsa kuuchotsa penateyo imene anamenya Richard Mbulu.

Zateremu mu gulu H ndiye kuti Flames ili pa nambala 6 ndi ma point 6, pamene Tunisia ikutsogolera gululi ndi ma point 16.

Related posts

Journalists urged to promote fair trading practices

Romeo Umali

Nsanje chiefs call for inclusion in environmental policies

Romeo Umali

Govt. boosts food security at Nkhata Bay Prison

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.