Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Sports Sports

Zavuta ku Tunisia!

Malawi yagonja 2-0 ndi Tunisia pa bwalo la masewero la Stade Olympique Hammadi Agebri munzinda wa Tunis. Awa anali masewero a mpira wamiyendo odzigulira malo mumpikisano wa 2026 World Cup.

Zigoli za Tunisia adamwetsa ndi Seifeddine Jaziri pamphindi 86 ndi Elias Achouri pamphindi 90+2 kudzera pa penote. Osewera wa Malawi, Lloyd Aarod, adapatsidwa Red Card mu mphindi 64.

Mwayi wa Flames unapezeka pa mphindi 90+8 kudzera pa penate koma ikakuona litsiro siikata, goloboyi wa Tunisia, Aymen Dahmen, anakwanitsa kuuchotsa penateyo imene anamenya Richard Mbulu.

Zateremu mu gulu H ndiye kuti Flames ili pa nambala 6 ndi ma point 6, pamene Tunisia ikutsogolera gululi ndi ma point 16.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Churches urged to reach out to those affected by hunger

Paul Mlowoka

Awanjata pogulitsa mankhwala owopsa

Blessings Kanache

Temwa aveka makanda pa chipatala cha Kamuzu Central

Tasungana Kazembe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.