Malawi Broadcasting Corporation
Agriculture Local Local News Nkhani

DoDMA igawa matani 4,000 achimanga kwa amene njala yawakhudza

Nthambi ya DoDMA yatsimikiza kuti ifikira anthu onse amene akhudzidwa ndi njala m’dziko muno.

M’modzi mwa akuluakulu ku nthambiyi, a Fyawupi Mwafongo, anena izi ku nkhokwe za chimanga ku Kanengo munzinda wa Lilongwe pamene amanyamula chimanga cha matani 4,000 kudzera pa stima yapamtunda, chimene akachigawe kwa anthu amene njala inawakhudza m’chigawo cha kummawa.

A Mwafongo ati DoDMA ndi yokonzeka kwambiri kuti ipereke chimanga Kwa anthu amene zovutazi zawakhudza ndipo akugwiritsa ntchito stima ya pamtunda komanso galimoto kuti akafikire anthuwa mu nthawi ya bwino.

Iwo anatinso ndi okondwa ndi kukonzedwanso kwanjanji m’dziko muno imene anati akunyamulirapo chimanga chochuluka pakamodzi ndi kufikira anthu mwa msanga komanso kupulumutsa ndalama zochuluka.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Malawi Prison partner NGOs to improve inmates’ well-being

MBC Online

Child injured as bus shelter collapses in Mangochi

MBC Online

First Lady urges action on education, youth poverty

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.