Malawi Broadcasting Corporation
Africa Crime Local Local News Nkhani

BOMA LATHETSA MULANDU WA OSOKONEZA MDIPITI

Boma lathetsa mulandu wa anthu atatu omwe anawamanga chifukwa chosokoneza mdipiti wa mtsogoleri wa dziko lino pa HHI mu mzinda wa Blantyre.

Mkulu oimira boma pa milandu, a Masauko Chamkakala, watsimikiza zankhaniyi polankhula ndi wailesi za MBC.

Anthu atatu omwe amawazenga mulanduwu, a Pearson Chimimba a zaka 48, a Hector Ndawala a zaka 38, komanso a Lucy Namba a zaka 35, anawamanga patapita masiku angapo, anthu omwe anali pa maliro ndipo amachokera dera lina ku Ndirande ndipo amapita kukaika zobvuta kumanda a HHI, atalimbana ndi apolisi a pamsewu kuti adutse msewu pa malowa.

Mtsogoleri wa dziko lino anali paulendo opita ku Chileka kukakwera ndege kupita ku Democratic Republic of Congo (DRC) pamene anthuwa anachita chisokonezochi.

#mbcnewslive
#mbconlineservices
#mbcnewslive

Related posts

SVTP to boost food security in Malawi – Govt

Rabson Kondowe

Mchinji embraces e-payment for social cash transfer

Rabson Kondowe

‘Connect A School Programme’ bridges digital divide in Dedza CDSSs

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.