Malawi Broadcasting Corporation
Business Local Local News Nkhani

‘Achinyamata akulephera kubweza ngongole za NEEF’

Bungwe la National Economic Empowerment Fund (NEEF) lati achinyamata sakubweza ngongole za bungweli moyenera akayerekeza ndi magulu ena amene akutenga ngongolezi.

Wapampando wa board ya bungweli, a Jephta Mtema, ndi amene ayankhula izi pa msonkhano umene bungweli linakonzera atsogoleri osiyanasiyana a munzinda wa Mzuzu ofotokoza mmene ngongoleyi ikuyendera.

Iwo ati achinyamata ambiri amakhala asanakhazikike muzochitika akamatenga ngongolezi ndipo nthawi yobweza amakhala kuti anasiya malonda komanso akuchita zina.

A Mtema ati achinyamata ena amakhala kuti alibe ukadaulo oyenereka oyendetsa malonda akamatenga ngongolezi ndipo amakhala akuphunzilira pa ngongoleyi.

Mfumu ya mzinda wa Mzuzu, a Kondwani Nyasulu, anati ngongole ya NEEF ili ndi kuthera kosintha miyoyo ya anthu akayigwiritsa bwino ntchito.

Olemba: Henry Haukeya

Related posts

Chakwera departs Maputo for 44th SADC Heads of State Summit in Harare

Alinafe Mlamba

Temwa Chawinga makes history as NWSL MVP

Rabson Kondowe

Sign language can develop Malawi — SLID

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.