Malawi Broadcasting Corporation
News Nkhani

Tilimbikitse ulimi wa mthilira – Kawinga

Ena mwa anthu 2000 opindula

Mtsogoleri wa Mpingo wa Salvation for All Ministries International, Apostle Clifford Kawinga, wati ulimi wa mthilira ungathandize dziko lino kukhala lodziyimira palokha pachakudya.

Apostle Kawinga anena izi pamene amagawa matumba a ufa komanso kulalikira uthenga wa Mulungu kwa nyezelera m’boma la Phalombe.

Iwo ati kusintha kwa nyengo kuphunzitse aMalawi kuyamba kupanga ulimi wamakono.

A Kawinga apempha mabungwe ndi mipingo kuti agwirane manja pothandiza anthu amene akhudzidwa ndi njala m’dziko muno.

Poyankhulapo, Paramount Chief Kaduya yati boma la Phalombe lakhudzidwa kwambiri ndi njala ndipo apempha akufuna kwabwino kuti athandize.

Olemba Blessings Cheleuka.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Allocate more funds to NEEF — CSO

Timothy Kateta

Plane crash investigations results to be made public

Beatrice Mwape

Silwimba Joins Wanderers

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.