Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Tigwirane manja pothana ndi cancer ya m’mawere – Udedi

Mwini wake wa kampani ya J.S Fitness ku Lilongwe, a Clement Udedi ati ndikofunika kuti aliyense atengepo gawo pothana ndi matenda a cancer ya m’mawere.

A Udedi anena izi pomwe anali ndi ulendo wa ndawala  komanso majowajowa munzinda wa Lilongwe omwe cholinga chake chinali kudziwitsa anthu za matendawa komanso kufuna kutolera ndalama zothandizira chimodzi mwa zipatala zing’onozing’ono zomwe zili mbali yaku Airwing munzindawu.

“Ngati JS Fitness gym tinaganiza kuti ife tichitepo mbali yathu. Tayenda ndipo tafalitsa uthenga ndipo tikudziwa kuti winawake wathandizika,” anatero a Udedi.

Bungwe loyang’anira za umoyo pa dziko lonse lapansi la World Health linakhazikitsa mwezi wa October ngati okumbukira za matenda a cancer ya m’mawere padziko lonse.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

‘Abambo akudzipha kwambiri kaamba kosowa upangiri’

Olive Phiri

Kalindo back in court for the firearm acquisition case

MBC Online

2023 survey reveals decline in banking services

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.