Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Tatumiza akatswiri woulutsa ma Drone — MUST

Chinthuzi: UNICEF

Sukulu ya za ukachenjede ya Malawi University  of Science and Technology (MUST) yatumiza akatswiri oulutsa tindege touluka tokha mlengamlenga kuti akathandize ndi ntchito yofunafuna ndege yomwe wakwera  wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino, Dr Saulos Chilima ndi anthu ena.

Ofalitsankhani wasukuluyi, a James Mphande, wauza MBC kuti tindegeti, tomwe timadziwika kuti ma Drones mchingerezi, tilipo toposa tisanu ndipo tikathandiza kwambiri chifukwa tidzikajambula dera lalikulu kwambiri mukanthawi kochepa.

A Mphande ati akatswiriwa anyamuka lero madzulo kupita m’chigawo chakumpoto.

Ndege yomwe wakwera wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko linoyu, yomwe inabwelera italephela kutera pa bwalo la ndege la Mzuzu, akuyiganizira kuti yasowa mu nkhalango ya Chikangawa chifukwa cha kuipa kwa nyengo.

 

 

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Elderly man drowns in well

Alinafe Mlamba

Respond to market needs – Gwengwe

MBC Online

Lotus plans Kayelekera Uranium Mine reopening

Yamikani Simutowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.