Malawi Broadcasting Corporation
Business Local Local News Nkhani

‘Sugar tsopano alipo ochuluka’

Anthu ambiri munzinda wa Blantyre ati ndi okondwa kwambiri kaamba kakuchuluka kwa sugar yemwe akupezeka m’masitolo komanso malo ochitira malonda ambiri.

Pakadali pano, mtengo wa sugar ukutsika komanso kukhazikika poyerekeza ndi momwe zinthu zinaliri masiku angapo apitawa chifukwa tsopano akugulitsidwa pa mitengo yapakati pa K2800 ndi K3000.

Chopatsa chidwi ndi chakuti ena mwa anthu ochita malonda omwe akhala akugulitsa sugar kunja kwa sitolo zina zikuluzikulu nawonso atsitsa mitengo yawo.

A Mirriam Chiwalo, amene amakhala ku Manyowe munzinda wa Blantyre, anati: “Panopa palibe kuchitira mwina koma kugulitsa sugar pa mtengo wa K3000 chifukwa choti wabwera wambiri mu sitolo ina yayikulu yomwe takhala tikumakagula ndi cholinga choti tidzigulitsanso kwa anthu ena.

“Zinthu tsopano zili bwino ndipo ndi zosangalatsa kwambiri kuti palibenso zokanganirana sugar monga momwe zinaliri padzana paja,” a Chiwalo adatero.

Posachedwapa, mkulu wa kampani ya Illovo Sugar, a Kondwani Msimuko, adanenetsa kuti katunduyu ayamba kupezeka mochuluka potsatira kuyambiranso kwa nyengo yogaya sugar.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Kaunda involved in motorcycle accident

Romeo Umali

Msukwa elected Chairperson of KA District Council

Rudovicko Nyirenda

Nkhata Bay communities hail Social Cash Transfer Programme

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.