Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Save The Children yapereka mbaula zamakono ku Lilongwe

Mabanja okwana makumi asanu ammudzi mwa mfumu yaikulu Masumbakhunda ozungulira khalango ya Dzalanyama m’boma la Lilongwe ali ndi chimwemwe atalandira mbaula zamakono zoyendera mphamvu ya dzuwa kuchokera ku bungwe la Save the Children.

Malinga ndi m’modzi mwa akuluakulu ku bungwel, a Bright Chidzumeni, kupereka mbaulazi ndi njira imodzi yochepetsa mavuto owononga nkhalango ya Dzalanyama, mmene anthu akhala akudulamo mitengo mopanda chilorezo ndicholinga chopanga nkhuni komanso makala ophikira.

M’modzi mwa anthu amene alandira nawo mbaulazi, a Lydia Banda, anati ithandiza kuchepetsa mchitidwe ogwiritsa ntchito ana kukafuna nkhuni ku nkhalangoyi popeza mbaulazi zimagwiritsa ntchito nkhuni zochepa.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Wanderers secure second place

Romeo Umali

‘Tidziyamba ndife aMalawi kutsatsa malonda a dziko lathu’

McDonald Chiwayula

Castel Malawi awards long-serving employees

Yamikani Simutowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.