Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Apolisi agwira ozembetsa makala komanso kulanda galimoto ku Blantyre

Apolisi m’chigawo chakumwera kuzambwe agwila amayi awiri komanso  bambo m’modzi chifukwa chopezeka ndi zinthu zaku nkhalango popanda chilolezo komanso kuzembetsa makala popanda zikalata zowayeneleza.

Malipoti omwe MBC yapeza asonyesa kuti komishonala wapolisi mchigawochi, a Noel Kaira, omwe anali limodzi

ndi maofesala awo kugwira ntchito yoyendera m’malo osiyanasiyana, usiku wa Lamulungu

anakumana ndi galimoto ya mtundu wa Scania pa roundabout ya Kameza.

Pokaikira zomwe inanyamula anayipanga chipikisheni ndipo anapeza kuti inali itadzadza ndi matumba a makala.

Apolisiwo anakwanitsa kugwira Samuel Ngwangwa, wochokera pamudzi wa  Chaswatheka, T/A Kunthembwe m’boma lomwelo la Blantyre, yemwe ndi dalaivala wa loleyo, a Merenia Chimtanda, wochokera pamudzi wa Dzikolatha, T/A  Mlauli, m’boma la Neno omwe amachita malonda komanso a  Mary Thuboyi,  wochokera pamudzi wa Chang’ambika, T/A Chapananga, m’boma la Chikwawa omwenso amachita bizinesi.

Kuyambira chaka, chatha apolisi alimbikitsa ntchito yoteteza zinthu zaku nkhalango pogwira limodzi ntchito ndi nthambi zosiyanasiyana, kuphatikizapo yaza nkhalango komanso yolimbana ndi mchitidwe wa ziphuphu ndi katangale ya Anti-Corruption Bureau.

Related posts

Malawi ramps up preparations for COP29

McDonald Chiwayula

YAS tells political parties to include youths in leadership positions

Romeo Umali

‘Protect Malawi’s environment’

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.