Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

President Dr Chakwera wayatsa magetsi a MAREP 9 ku Luviri

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera wayatsa magetsi pa sitolo za Luviri m’boma la Mzimba muntchito yopereka magetsi akumudzi ya MAREP.

Luviri ndi imodzi mwa ma trading centre 13 amene akulandira magetsi mu ntchito yachisanu ndi chinayi (9) yopereka magetsi kumidzi.

Pakadali pano, mabanja okwana 50 mwa 250 omwe anayerekeza kuti apeza magetsiwa alandira kale kuderali.

Malinga ndi nduna yowona za mphamvu za magetsi, a Ibrahim Matola, boma lapeza ndalama zoposa €70 million zomwe zithandizire kuika mapolo achitsulo kuchoka ku Nkhoma Power Station ku Lilongwe kufika m’chigawo cha kumpoto.

Dr Chakwera, amene ali pa ulendo opita ku chigawo cha kumpoto, anaima kucheza ndi anthu amene anali mu njira, kudikilira kuti awaone.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Boma lipitiriza kumamvana ndi ma Bishopu a Katolika

Blessings Kanache

Malaulo: Anjatidwa atagwililira mwana omupeza pofuna kukhwima

Charles Pensulo

Unduna oona za madzi wati upitilira kupereka madzi abwino

Beatrice Mwape
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.