Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

President Chakwera ayamikira ntchito yokonza msewu wa M1

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera wati ndiokhutira ndi momwe ikuyendera ntchito yokonzanso msewu wa M1.

Dr Chakwera anena zimenezi pa Mtengowanthenga pomwe analankhula kwa nantindi wa anthu amene asonkhana.

Dr Chakwera anati anaganiza  zodutsa mu msewu wa M1 popita ku Mzuzu, kuti awone yekha ntchitoyo.

Iwo anatsimikiziranso anthu kuti ntchito yokonza dzikoli ili mkati, kuti mibadwo ikubwerayi idzakhale ndi dziko labwino, ndipo anayamika anthu aku Dowa chifukwa ndi olimbika pa ntchito.

Mtsogoleri wa dziko linoyu anati nkofunika kuti dziko la Malawi likhale lodzidalira osati lopempha pempha.

“Komanso tiyeni tisamalire ntchito zachitukuko zomwe tili nazo, osaononga ayi ” anatero Dr Chakwera.

 

Olemba: Isaac Jali

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Nditha kusiyira sukulu panjira — Mphatso

Blessings Kanache

Govt handover houses to persons with Albinism

MBC Online

CS-EPW participants tipped on small scale businesses

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.