Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Owona zaumoyo atulutsa zotsatira zonse za ‘ambuye tengeni’ mu sabata ziwiri

Akuluakulu owona zaumoyo ku Blantyre ati atulutsa kumapeto a sabata ziwiri zikubwerazi zotsatira za kafukufuku wa chenicheni chomwe chinali mu mowa omwe wapha anthu okwana asanu ndi atatu mu mzindawu.

Malinga ndi mkulu wa mu office yowona zaumoyo ku Blantyre, Dr Gift Kawalazira, pakadali pano akatswiri odziwa zakafukufuku pachipatala chachikulu Cha Queens Ali mkati mounika mozama pa zinthu zomwe zinali mu mowawu.

Polankhula mu programme ya the Pot ku MBC, a Kawalazira anatinso office ya zaumoyo ku Blantyre mogwirizana ndi nthambi komanso mabungwe ena akhala akuyendera madera wosiyanasiyana pofuna kuzindikiritsa anthu zakuopsa komwa mowa wosadziwika bwinowu.

 

Olemba Timothy Kateta

Related posts

FIVE DIE OF SUSPECTED ALCOHOL POISONING

Romeo Umali

BWALO LA MILANDU LABWEZA GALIMOTO YA UMBONI WABOMA

Romeo Umali

Farmers regain hope in Mutharika’s first 100 days

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.