Unduna wa zamaphunziro walangiza ophunzira omwe ali ndi ulumali kuti asamadziyang’anire pansi chifukwa nawo ali ndi kuthekera kochita bwino.
M’neneri ku undunawu, a Mphatso Mkuonera, amayankhula izi m’boma la Kasungu pamene amayendera ntchito yomanga zipinda zophunzilira, za sayansi komanso zowerengerako mabukhu zomwe zili pansi pa ntchito ya Equity with Quality Learning at Secondary (EQUALS).
Atafika pa Sekondale ya Kasungu, a Mkuonera anakumana ndi achinyamata amene ali ndi khungu la chi alubino ndipo iwo anati boma likumanga zithu zambiri zokhudza maphunziro zomwe ndi zokomera onse m’dziko muno pakusatengera ulumali.
Ntchito ya EQUALS ikulandira thandizo kuchokera ku World Bank.