Malawi Broadcasting Corporation
Education Local Local News Nkhani

Ophunzira a ulumali asamadziyang’anire pansi — Mkuonera

Unduna wa zamaphunziro walangiza ophunzira omwe ali ndi ulumali kuti asamadziyang’anire pansi chifukwa nawo ali ndi kuthekera kochita bwino.

M’neneri ku undunawu, a Mphatso Mkuonera, amayankhula izi m’boma la Kasungu pamene amayendera ntchito yomanga zipinda zophunzilira, za sayansi komanso zowerengerako mabukhu zomwe zili pansi pa ntchito ya Equity with Quality Learning at Secondary (EQUALS).

Atafika pa Sekondale ya Kasungu, a Mkuonera anakumana ndi achinyamata amene ali ndi khungu la chi alubino ndipo iwo anati boma likumanga zithu zambiri zokhudza maphunziro zomwe ndi zokomera onse m’dziko muno pakusatengera ulumali.

Ntchito ya EQUALS ikulandira thandizo kuchokera ku World Bank.

 

Print Friendly, PDF & Email

Author

  • Mayeso Chikhadzula joined MBC in 2006, he's an Investigative Journalist and Principal Reporter. He's also a News Anchor, Presenter, and producer.

Related posts

Akupha makwacha ndi bizinesi ya tiyi lumu ku Lilongwe

MBC Online

MACRA ALLOCATES NEW FM FREQUENCIES

MBC Online

Chakwera arrives in Lusaka ahead of the SADC Extraordinary Summit of Organ Troika

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.