Malawi Broadcasting Corporation
Health Local Local News Nkhani

‘Odwala sakumadya mokwanira’

Komiti ya nyumba ya malamulo yoona zaumoyo yati zipitala zambiri zikulephera kupereka chakudya mokwanira kwa odwala chifukwa cha kuchepekedwa kumbali ya ndalama.

Wapampando wa komitiyi, a Matthews Ngwale, ananena izi m’nyumbayi pamene amapereka lipoti lokhudza kaperekedwe ka chakudya kwa odwala m’zipatala za m’dziko muno.

A Ngwale anati aphungu a komiti yawo anayendera zipatala za maboma a Thyolo, Balaka, Dowa, Rumphi komanso Ntcheu pamene amafuna kukaona m’mene nkhani yopereka chakudya kwa odwala ikuyendera.

Chipatala cha Mzimba chokha akuti ndi chimene chikukwanitsa kupereka chakudya katatu patsiku.

Komitiyi yapempha boma kuti lidzipereka ndalama zokwanira komanso mu nthawi yake kuti mavutowa achepe.

Related posts

Portland can generate forex — Tembo

Romeo Umali

PRIORITISE EXPERIENCED TECHNICAL PANELS FOR LEAGUE SURVIVAL — ANALYST

Romeo Umali

Irish Ambassador donates K5.3 million for Paris 2024 Paralympics

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.