Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Mpingo wa CCAP walandira a Moses Kunkuyu m’gulu la Utumiki wa Abambo

Synod ya Blantyre ya Mpingo wa CCAP tsopano yaonjezera chiwerengero cha abambo omwe ndi mamembala a Utumiki wa Abambo, potsatira kupatulidwa kwa gulu la abambo omwe awalandira ku mpingo wa Manase CCAP mu mzinda wa Blantyre.

Nduna ya zofalitsa nkhani omwenso ndi mneneri wa boma a Moses Kunkuyu ndi mmodzi mwa mamembala atsopano a Utumiki wa a Bambo mu Synod ya Blantyre.

Polankhula pa mwambo opatula mamembala atsopanowo, m’busa Evance James Kapulula omwe amatumikira pa Manase CCAP anati kukhala ndi membala wa Utumiki wa Abambo yemwenso ndi nduna ya boma ndi chisonyezo chachikulu pa kudalirana komwe kulipo pakati pa mpingo ndi boma pa ntchito yosamalira a Malawi.

A Kunkuyu omwe anakhalako Mlembi wa mpingo wa Manase CCAP kawiri ati kupatulidwa kwawo n’kukhala mu Utumiki wa Abambo kwapereka

chilimbikitso pa ntchito yotumikira pa Chikhristu mu Synod ya Blantyre.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Govt calls for multi-sectoral approach in scaling up clean energy

Mayeso Chikhadzula

Athana ndi umphawi pokonza sopo

Doreen Sonani

MPs commend Chakwera for fostering youth empowerment

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.