Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Mnyamata wazaka 18 wapambana ku Misuku

Hope Msukwa, amene ndi wa zaka 18, wapambana pa mpikisano okwera njinga zamoto kumapiri aku Misuku m’boma la Chitipa.

Iyeyu wapambana atayendetsa njinga yamoto kwa mphindi 47 pa mtunda wama kilometre 48 ndipo wapeza mphoto ya K1.4 million komanso wagonjetsa anyamata ena oposa 49 amene amapikisana nawo.

Hope anati agwiritsa ntchito ndalamayo kuti agule njinga yake chifukwa imene amagwiritsa ntchito pa mpikisanowo ndi yobwereka.

Thokozani Kanyika ndi amene wakhala wachiwiri ndipo walandira K900,000 pamene Zakaria Kaini wathera pachitatu ndipo walandira K615,000.

Olemba: Hassan Phiri

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Serve Malawians, Chakwera advises Mumba

Chisomo Manda

MEC to announce nomination fees next month

Austin Fukula

Dr Chakwera ayamikira anthu ku Nsanje posamukira kumtunda

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.