Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani

Mlimi watola chikwama

Mlimi wa ku Blantyre, a Mariko Kalima, wayiphula pamene wapata K2.5 million mu mpikisano wa Tisanje umene ikupangitsa ndi kampani yopanga sopo ya Hirwa General Dealers.

Polankhula pamene kampaniyi imapereka mphothoyi ku Ndirande munzinda wa Blantyre, kudzera kwa kazembe wawo, Emmie Deebo, a Kalima anathokoza kampaniyi ponena kuti ndalama iwathandiza pogula fetereza ndi zipangizo zina za kumunda.

Mkulu owona za malonda ku kampaniyi, a Best Balala, anati anakhazikitsa mpikisanowu pofuna kuthandiza makasitomala awo mu nthawi ino pamene chuma chikuvuta.

Related posts

Government lauds CSAT for enhancing citizen governance

MBC Online

MARANATHA RELOCATES TEMPORARILY

MBC Online

DODMA needs K209 billion to reach out to those affected by food insecurity

Alinafe Mlamba
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.