Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

‘Mgwirizano ndi ofunika pa ntchito yobwezeretsa chilengedwe’

Bwanamkubwa wa boma la Neno, Rosemary Nawasha, wati adindo m’bomalo akugwilira ntchito limodzi pofuna kuthana ndi mchitidwe owononga zachilengedwe komanso kubwezeretsa chilengedwe .

A Nawasha ayankhula izi pa sukulu ya pulaimale ya Chikonde pomwe khonsolo ya bomali imalipira anthu omwe akugwira ntchito za m’bwezera chilengedwe yomwe imadziwika kuti Climate Smart Enhanced Public Works Programme (CSEPWP) mchingerezi.

Iwo alangiza anthu omwe akugwira ntchitoyi kuti adzigwiritsa ntchito ndalama zomwe akulandirazo mwa dongosolo kuti miyoyo yawo itukuke.

M’boma la Neno, anthu oposa 14,000 ndiwo akugwira ntchitoyi mmadera khumi ndi anayi.

Anthuwa adzilandira K38,400 pakutha masiku 24.

Mwa zina mu ntchitoyi  anthuwa akumadzala mitengo komanso kuchita akalozera mmunda pofuna kuteteza kukokoloka kwa nthaka.

 

Olemba: Naomi Kamuyango

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Government launches Agricultural Diversification, Commercialisation booklet

MBC Online

MUBAS urges joint efforts for digital transformation

MBC Online

Southern Region Anglican Church promotes youth empowerment

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.