Malawi Broadcasting Corporation
Crime Local Local News Nkhani

Mayi amunjata pofuna kulowetsa chamba kundende

Apolisi munzinda wa Zomba amanga a Jessie Mpanira, 35, powaganizira kuti amafuna kulowetsa chamba ku ndende ya Zomba Maximum.

Wachiwiri kwa ofalitsa nkhani za polisi ya Zomba, a Andrew Mwale, ati mayiyu anapita ku ndendeko kuti akawone mulamu wake amene akugwira ukayidi kwa moyo wake wonse.

Malinga ndi a Mwale, mayiyo anatenga nsima imene anabisamo fodya wamkuluyo.

Monga mwa malamulo, oyang’anira pa ndendepo anayamba kuyiwunika nsimayo asanakayipereke ndipo anazindikira kuti mayi Mpanira anabisa chamba mkati mwa nsimayo.

Amene akuwaganizirawa ndi a m’mudzi wa Duncan, mfumu yayikulu Malemia m’boma la Zomba.

 

Related posts

MDF says culture unites military officers

Alinafe Mlamba

Tea Association projects more produce this year

Romeo Umali

Super League soldiers fall

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.