Malawi Broadcasting Corporation
Culture Development Local Local News Nkhani

Mafumu ayamikira ndondomeko yolembetsa malo

Mafumu a m’boma la Blantyre ayamikira boma pokhazikitsa ntchito yolembetsa umwini wa malo.

Mfumu yayikulu Kunthembwe inati ntchito yolembetsa maloyi ndi yabwino kwambiri kaamba kakuti ichepetsa ziwawa zimene zimabwera chifukwa cha kusamvana pa nkhani zokhudza malo.

Iwo amayankhula izi pa msonkhano wapakati pa unduna wa zamalo ndi mafumu okhala m’mbali mwa mtsinje wa Shire.

Mkulu oona za zantchito kuunduna wa zamalo, a Dr Victor Sandikomda, anati mafumu ndi ofunika kuti amvetse bwino malamulo atsopano a malo chifukwa iwo ndi eni nthaka.

Ntchitoyi ikutheka ndi thandizo lochokera ku bungwe la Malawi Watershed Services Improvement Project.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Social Cash Transfer Programme to register 361,642 new beneficiaries

MBC Online

Mlembi wamkulu wa Synodi akhetsa msozi ku msonkhano waukulu

MBC Online

2024 MW Investment & Trade Forum cancelled

Earlene Chimoyo
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.