Malawi Broadcasting Corporation
Culture Development Local Local News Nkhani

Mafumu ayamikira ndondomeko yolembetsa malo

Mafumu a m’boma la Blantyre ayamikira boma pokhazikitsa ntchito yolembetsa umwini wa malo.

Mfumu yayikulu Kunthembwe inati ntchito yolembetsa maloyi ndi yabwino kwambiri kaamba kakuti ichepetsa ziwawa zimene zimabwera chifukwa cha kusamvana pa nkhani zokhudza malo.

Iwo amayankhula izi pa msonkhano wapakati pa unduna wa zamalo ndi mafumu okhala m’mbali mwa mtsinje wa Shire.

Mkulu oona za zantchito kuunduna wa zamalo, a Dr Victor Sandikomda, anati mafumu ndi ofunika kuti amvetse bwino malamulo atsopano a malo chifukwa iwo ndi eni nthaka.

Ntchitoyi ikutheka ndi thandizo lochokera ku bungwe la Malawi Watershed Services Improvement Project.

Related posts

NEEF urges persons with disabilities in Chitipa to access loans

MBC Online

SUSPECT IN ALLAN WITTIKA MURDER CASE TO APPEAR IN COURT

MBC Online

MPs await Leader of Opposition’s evidence on vote rigging allegations

McDonald Chiwayula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.