Malawi Broadcasting Corporation
Development Education Local Local News Nkhani

Madam Chakwera atsegula sukulu ya Chiyola CDSS

Mayi wa pfuko lino, Madam Monica Chakwera, atsegulira sukulu yatsopano ya sekondale yoyendera ya mdera la Chiyola m’boma Rumphi imene bungwe la Press Trust lamanga.

Sukuluyi ili ndi zipinda zofunika monga makalasi ophunzirira ngakhalenso chipinda chosungira mabuku.

Themba la Mathemba Chikulamayembe athokoza boma popititsa patsogolo maphunziro m’dziko muno ndipo ati chiyembekezo kuti derali litukuka kwambiri m’magawo osiyanasiyana chifukwa cha sukuluyi.

Iwo atinso atsikana mderali amayenda mtunda wautali kuti akapeze maphunziro ku sukulu za Mwasizi ngakhalenso Katowo.

Related posts

Judiciary launches financial crimes division

Rabson Kondowe

SDA CHURCH AWARDS COMMUNICATORS

Alinafe Manong'a

Govt receives K6.4 Billion in second phase of Fleming Fund

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.