Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Kamtukule alowa chipani cha MCP

Nduna ya zokopa alendo a Vera Kamtukule omwe anali achipani cha UTM alowa chipani cha Malawi Congress.

Powalandira mchipanichi Mlembi Wamkulu mchipani cha MCP a Eisenhower Mkaka ati a Kamtukule sanasochere kaamba koti alowa chipani chomwe chilibe mwini koma mchipani cha m’Malawi aliyense.

A Mkaka ati chipani cha MCP chili chokonzeka kulandira aliyense yemwe watsimikiza mtima kulowa chipanichi.

Poyankhulapo a Kamtukule ati alowa chipanichi kaamba koti akufuna kuthandiza mtsogoleri wadziko lino  Dr Lazarus Chakwera pogwira ntchito yotukula dziko la Malawi.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Scorchers Goalie nominated for COSAFA Awards

MBC Online

Chimwendo praises MCP unity ahead of 2025 elections

MBC Online

Youths are vital to achieving Malawi 2063 — Kazombo

Mayeso Chikhadzula
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.