Malawi Broadcasting Corporation
Development Local Local News Nkhani

Immigration, ACB akufuna kuthetsa ziphuphu

Bungwe la Immigration lati pakufunika mgwirizano polimbikitsa aMalawi kuti azitsata malamulo pamene akupita maiko ena.

M’modzi mwa adindo ku bungweli, a Fletcher Nyirenda, anayankhula izi pamasewero osiyanasiyana amene Immigration inakonza ku Lilongwe.

Oona ntchito zothana ndi katangale ku bungwe la Anti-Corruption Bureau (ACB), a Susan Mtuwa Phiri, anali komweko ndipo anaphunzitsa anthu ogwira ntchito ku Immigration zokhudza ziphuphu ndi katangale.

A Phiri anati izi zili chomwechi chifukwa m’chitidwe wa ziphuphu ndi katangale umachitikanso kunthambi zaboma.

Iwo anati ubale wanthambi ziwirizi usangokhala omanga anthu koma wothandizana kupewa m’chitidwe oyipawu kuchitika.

Malipoti akuonetsa kuti nzika zina za dziko lino zakhala zikugwidwa m’dziko la South Africa kaamba kosowa mapepala owayenereza opitira kumeneko.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

KABAMBE OFFICE ABUSE CASE TO COMMENCE AUGUST 15

McDonald Chiwayula

UNDUNA WAZA CHUMA UKULINGALILA ZOONJEZELA NDALAMA KUBUNGWE LA NEEF

MBC Online

BT to host Kamuzu Day celebrations

Eunice Ndhlovu
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.