Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Flames yakale isewera ndi Zambia yakale

Flames ya osewera akale idzasewera ndi timu ya osewera akale a m’dziko la Zambia mwezi wa mawa m’dziko muno.

Membala wa board ya bungwe la osewera akalewa la Football Legends Association, a Rashid Ntelera, wati padakali pano akukonzekera masewerowo kuti adzakhale apamwamba ndi achikoka.

Awa adzakhala masewero achibwereza chifukwa Malawi inagonja ndi zigoli ziwiri kwa chimodzi mu masewero oyamba ku Zambia chaka chatha.

Clifford Mulenga komanso Ignicious Lwipa anamwetsa zigoli za Zambia pamene Jimmy Zakazaka ndi amene anagoletsera Malawi.

Bungwe la Football Legends Association, lomwe anayambitsa ndi a Jim Kalua, linabweretsa pamodzi osewera komanso oyendetsa mpira akale ndipo pakadali pano lili ndi mamembala opitilira 124.

Olemba: Amin Mussa

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Former Flames goalie no more

Romeo Umali

Chakwera to attend trade and investment forum in Bahamas

Kumbukani Phiri

Malawi appeals for more funding from AFDB to accelerate Development amid economic hurdles

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.