Malawi Broadcasting Corporation
Local Local News Nkhani Sports Sports

Flames yakale isewera ndi Zambia yakale

Flames ya osewera akale idzasewera ndi timu ya osewera akale a m’dziko la Zambia mwezi wa mawa m’dziko muno.

Membala wa board ya bungwe la osewera akalewa la Football Legends Association, a Rashid Ntelera, wati padakali pano akukonzekera masewerowo kuti adzakhale apamwamba ndi achikoka.

Awa adzakhala masewero achibwereza chifukwa Malawi inagonja ndi zigoli ziwiri kwa chimodzi mu masewero oyamba ku Zambia chaka chatha.

Clifford Mulenga komanso Ignicious Lwipa anamwetsa zigoli za Zambia pamene Jimmy Zakazaka ndi amene anagoletsera Malawi.

Bungwe la Football Legends Association, lomwe anayambitsa ndi a Jim Kalua, linabweretsa pamodzi osewera komanso oyendetsa mpira akale ndipo pakadali pano lili ndi mamembala opitilira 124.

Olemba: Amin Mussa

Related posts

Nditha kusiyira sukulu panjira — Mphatso

Blessings Kanache

President Chakwera to attend Sub-Region Catholic Bishops conference

Romeo Umali

Legal Aid Bureau has 25, 000 active cases

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.