Malawi Broadcasting Corporation
Nkhani

Dr Chakwera apereka K5 million zothandizira pamaliro a Kasambara

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera wapereka ndalama zokwana K5 million kuti zithandizire pamwambo wa maliro a Raphael Kasambara omwe atisiya masiku apitawa.

A Harry Mkandawire, amene akuyimira Dr Chakwera, ati malemu a Raphael Kasambara anali munthu okonda kumenyera ufulu wa anthu osauka.

Iwo ati boma lisowa ntchito zambiri zomwe malemuwa anathandizirapo maaka pa chitukuko.

A Mkandawrire ayankhula izi pamene mwambo wa maliro uli mkati m’boma la Nkhata Bay.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Malawi ndi bwenzi lenileni la dziko la Zambia — Lufuma

Mayeso Chikhadzula

Madam Chakwera ayamikira Press Trust potukula maphunziro

Beatrice Mwape

MACRA ikufuna mtengo wa ‘smartphone’ utsike

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.