Malawi Broadcasting Corporation
Entertainment Local Local Music News Nkhani

Chimbale chatsopano ndichothokoza Mulungu — Thuya

Oyimba nyimbo za uzimu, mayi busa Mary Thuya, ati chimbale chimene akutulutsa chotchedwa “Ndathokoza” ayimba pothokoza Mulungu kaamba kowachiritsa ku matenda a Covid-19.

A Thuya anena izi pokonzekera mwambo okhazikitsa chimbalechi, umene udzakhalepo Lamulungu likudzali munzinda wa Lilongwe.

Iwo ati anthu amene adzapite kumwambowu ayembekezere kukalimbikitsika kudzera ku umboni wawo.

Oyimba ena amene akaimbe nawo ndi monga Sir Norman Phiri, Favoured Martha, Alex Nkalo, Milefa Sisters komanso Maxwell Oloto.

 

Related posts

Motorists charged extra to fuel vehicles in Balaka

Romeo Umali

NCST sets high expectations on Academy of Sciences

Alinafe Mlamba

Education Ministry for smooth MANEB exams

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.