Malawi Broadcasting Corporation
Local News Nkhani

Chenjerani namondwe akhoza kubuka panyanja yamchere

Nthambi yoona zanyengo m’dziko muno yachenjeza kuti namondwe akhoza kubuka lamulungu lino panyanja yamchere pakati pa mayiko a Madagascar ndi Mozambique ndipo ali ndikuthekera kofalikira m’chigawo chakummwera kwa dziko lino.

Kudzera mukalata imene nthambiyi yatulutsa, iyo yatinso madera ambiri apitilira kulandira mvula yochuluka ndipo yalangiza anthu kuti apewe kuwoloka mitsinje yodzadza ndikukhala tcheru chifukwa madzi akhoza kusefukira madera ochuluka.

Izi zikudza pamene madzi osefukira asautsa anthu mmaboma a Nkhotakota ndi Karonga.

Mtsogoleri wa dziko lino Dr Lazarus Chakwera akuyembekezeka kuyendera ena mwa anthuwa ku Dwangwa m’boma la Nkhotakota.

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Dr Chakwera to inspect Kholongo Dam

MBC Online

Baka City FC registers first win in TNM Super League

Rudovicko Nyirenda

Malawi’s first State of the Map conference calls for tech innovation

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.