Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Band yanyimbo zauzimu yadziko lonse ibwera poyera

Gulu la akatswiri oyimba nyimbo zauzimu  osachepera 50 amene adakumana koyamba mu 2020, tsopano akhazikitsa Hephzibah Worship Band.

Malinga ndi mkulu wa gululi a Peterson Nachanje, cholinga cha gululi ndi kusula komanso kutukula luso lamayimbidwe auzimu.

“Sitikusiyana kwenikweni ndi Joyous Celebration yaku South Africa. Sitikuona mpingo koma luso lamunthu, kaya amatha kuimba zida kaya mawu, ali olandiridwa abwere,” atero a Nachanje.

M’modzi mwa otsogolera gululi ndi Good Friday, yemwe anatchuka ndi nyimbo yoti ‘Wanga ndili Naye’ ndipo wati gululi linayamba kujambula chimbale m’chaka cha 2021 ndipo pofika lero lajambula akanema atatu apamwamba.

 

Wolemba: Emmanuel Chikonso

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

TRADE programme calls for sustainable livestock farming

Jeffrey Chinawa

Man drowns while stealing fish in Lake Malombe

Davie Umar

E-ticketing can promote accountability among festival organisers – TNM

MBC Online
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.