Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Band yanyimbo zauzimu yadziko lonse ibwera poyera

Gulu la akatswiri oyimba nyimbo zauzimu  osachepera 50 amene adakumana koyamba mu 2020, tsopano akhazikitsa Hephzibah Worship Band.

Malinga ndi mkulu wa gululi a Peterson Nachanje, cholinga cha gululi ndi kusula komanso kutukula luso lamayimbidwe auzimu.

“Sitikusiyana kwenikweni ndi Joyous Celebration yaku South Africa. Sitikuona mpingo koma luso lamunthu, kaya amatha kuimba zida kaya mawu, ali olandiridwa abwere,” atero a Nachanje.

M’modzi mwa otsogolera gululi ndi Good Friday, yemwe anatchuka ndi nyimbo yoti ‘Wanga ndili Naye’ ndipo wati gululi linayamba kujambula chimbale m’chaka cha 2021 ndipo pofika lero lajambula akanema atatu apamwamba.

 

Wolemba: Emmanuel Chikonso

Related posts

Malawians will enjoy ECF benefits, says Gwengwe

Rabson Kondowe

Consumers urged to use proper channels for complaints – MACRA

McDonald Chiwayula

Bungwe la MEC layamba kuonkhetsera zotsatira za chisankho kumsonkhano waukulu wachipani cha DPP

Rabson Kondowe
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.