Malawi Broadcasting Corporation
News

Anthu 1,200 alandira matumba achimanga ku Balaka

Mtsogoleri wa Mpingo wa Salvation for All Ministries International, m’busa Clifford Kawinga, wapempha mabungwe ndi amipingo kuti agwirane manja pothandiza anthu omwe akhudzidwa ndi njala m’dziko muno.

A Kawinga anena izi pamene amagawa matumba achimanga kwa anthu 1,200 komanso kulalikira uthenga wa Mulungu m’dera la mfumu yaikulu Matola m’boma la Balaka.

M’busayu wati apitiliza kutumikira anthu powalalikira komanso kuthandiza zosowa zawo za thupi.

Iwo anagawanso ma Baibulo kwa mafumu ndi atsogoleri osiyanasiyana.

 

Wolemba: Blessings Cheleuka

Related posts

NICO doubles sponsorship for National Schools Chess League

Rabson Kondowe

Mobile network provider welcomes MACRA’s certification system

Rabson Kondowe

Kusankhidwa kwa Justice Mtalimanja kulimbikitsa atsikana, amayi — Undule

Romeo Umali
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.