Malawi Broadcasting Corporation
Local Nkhani

Amumanga pomuganizira kuti wapha mkazi wake chifukwa cha nsanje

Chataika Makawa wazaka 45 ali mchitokosi cha polisi ku Mangochi pomuganizira kuti wapha mkazi wake Esimy Daudi wazaka 42, amene amamukayikira kuti anali ndi chibwenzi.

Ofalitsankhani za polisi ya Mangochi, Amina Tepani Daudi, wati Makawa amumanga mmudzi mwa Kwitunji mdera la mfumu yaikulu Katuli dzulo pomuganizira kuti wapha mkazi wakeyo pomubaya ndi chikwanje kumsana.

Daudi wati mukafukufuku wawo, apolisi apeza kuti banjali linali lapendapenda chifukwa mamunayu amamulonda kwambiri mkaziyo pomuganizira kuti amayenda njila zamseli.

Makawa akaonekera ku khothi kukayankha mlandu wakupha.

 

Print Friendly, PDF & Email

Related posts

Media must accurately report on Mwanza Border — MRA

Timothy Kateta

MultiChoice assures fans of FA Community Shield coverage

Blessings Kanache

Ana 169 apulumutsidwa ku maukwati

Lonjezo Msodoka
error: All Content is protected. Copyright © 2022. Malawi Broadcasting Corporation. All Right Reserved.